Kodi Mungakonde Kudziŵa Zambili?
Munthu wina wanzelu analemba kuti: “Nzelu ndiyo cinthu cofunika kwambili. Peza nzelu, ndipo pa zinthu zonse zimene upeze, upezenso luso lomvetsa zinthu.” (Miyambo 4:7) Mlengi wathu amatiphunzitsa kuti tikhale anzelu komanso omvetsa zinthu n’colinga cakuti tizipanga zisankho zabwino na kukhala na umoyo wacimwemwe.
Kuti mudziŵe zambili zokhudza malangizo anzelu a m’Baibo, pitani pa jw.org. Pamenepo mudzapeza . . .
BAIBO
MAVIDIYO
MAVIDIYO A TUKADOLI
MBALI ZA KUFUNSA MAFUNSO
NKHANI
Zonsezi ni zaulele, ndipo zimathandiza anthu a misinkhu yosiyana-siyana komanso a zikhalidwe zosiyana-siyana.