Wolembedwa ndi Maliko 12:1-44

  • Fanizo la alimi amene anapha anthu (1-12)

  • Mulungu komanso Kaisara (13-17)

  • Funso lokhudza kuuka kwa akufa (18-27)

  • Malamulo awiri aakulu kwambiri (28-34)

  • Kodi Khristu ndi mwana wa Davide? (35-37a)

  • Anawachenjeza kuti asamale ndi alembi (37b-40)

  • Timakobidi tiwiri ta mayi wamasiye wosauka (41-44)

12  Kenako anayamba kulankhula nawo pogwiritsa ntchito mafanizo kuti: “Munthu wina analima munda wa mpesa+ nʼkumanga mpanda kuzungulira mundawo. Komanso anakumba dzenje loponderamo mphesa nʼkumanga nsanja.+ Atatero anausiya mʼmanja mwa alimi nʼkupita kudziko lina.+  Ndiye nyengo ya zipatso itakwana, anatumiza kapolo wake kwa alimiwo kuti akamupatseko zina mwa zipatso zamʼmunda wa mpesawo.  Koma iwo anamugwira nʼkumumenya ndipo anamubweza chimanjamanja.  Iye anatumizanso kapolo wina kwa iwo koma ameneyu anamutema mʼmutu komanso kumuchitira zachipongwe.+  Anatumizanso wina koma ameneyo anamupha. Ndiyeno anatumizanso akapolo ena ambiri. Ena mwa iwo anawamenya ndipo ena anawapha.  Iye anatsala ndi mmodzi yekha woti amutumize, mwana wake wokondedwa.+ Choncho anamutumizadi nʼkunena kuti, ‘Mwana wanga yekhayu akamulemekeza.’  Koma alimiwo anayamba kukambirana kuti, ‘Eyaa! uyu ndi amene adzalandire cholowa.+ Bwerani, tiyeni timuphe ndipo cholowacho chidzakhala chathu.’  Choncho anamugwira nʼkumupha ndipo anamutulutsa mʼmunda wa mpesawo.+  Kodi mwiniwake wa mundawo adzachita chiyani? Iye adzabwera nʼkupha alimiwo ndipo munda wa mpesawo adzaupereka kwa ena.+ 10  Kodi simunawerengepo zimene lemba limanena? Paja limanena kuti: ‘Mwala umene omanga nyumba anaukana wakhala mwala wapakona wofunika kwambiri.*+ 11  Umenewu wachokera kwa Yehova* ndipo ndi wodabwitsa mʼmaso mwathu.’”+ 12  Atamva zimenezo ankafuna kumugwira,* koma anaopa gulu la anthu, chifukwa iwo anadziwa kuti iye ananena fanizolo akuganiza za iwowo. Choncho anangomusiya nʼkuchokapo.+ 13  Pambuyo pake anamutumizira ena mwa Afarisi ndi anthu amene ankatsatira Herode kuti akamupezere zifukwa pa zimene angalankhule.+ 14  Atafika, iwo anamuuza kuti: “Mphunzitsi, tikudziwa kuti inu mumanena zoona ndipo simuchita zinthu pongofuna kusangalatsa munthu, chifukwa simuyangʼana maonekedwe a anthu, koma mumaphunzitsa njira ya Mulungu mogwirizana ndi choonadi. Kodi nʼzololeka* kupereka msonkho kwa Kaisara kapena ayi? 15  Kodi tizipereka kapena tisamapereke?” Yesu anazindikira chinyengo chawo ndipo anawafunsa kuti: “Bwanji mukundiyesa? Bweretsani khobidi la dinari* kuno ndilione.” 16  Iwo anamubweretsera ndipo iye anawafunsa kuti: “Kodi nkhope iyi komanso mawu akewa nʼzandani?” Iwo anayankha kuti: “Ndi za Kaisara.” 17  Choncho Yesu ananena kuti: “Perekani zinthu za Kaisara kwa Kaisara,+ koma za Mulungu kwa Mulungu.”+ Ndipo iwo anadabwa naye kwambiri. 18  Kenako Asaduki amene amanena kuti akufa sadzaukitsidwa,+ anabwera nʼkumufunsa kuti:+ 19  “Mphunzitsi, Mose anatilembera kuti ngati mwamuna wamwalira nʼkusiya mkazi koma osasiya mwana, mchimwene wake akuyenera kutenga mkazi wamasiyeyo nʼkuberekera mchimwene wake uja ana.+ 20  Ndiyeno panali amuna 7 apachibale. Woyamba anakwatira mkazi, koma anamwalira alibe ana. 21  Wachiwiri anakwatira mkaziyo, koma nayenso anamwalira osasiya mwana. Zinachitikanso chimodzimodzi kwa wachitatu. 22  Ndipo onse 7 aja sanasiye mwana. Pamapeto pake mkazi uja anamwaliranso. 23  Kodi pamenepa, akufa akadzaukitsidwa mkazi ameneyu adzakhala wa ndani? Popeza onse 7 anamukwatira.” 24  Yesu anawayankha kuti: “Mukulakwitsa. Kodi kulakwitsa kumeneku si chifukwa chakuti simudziwa Malemba kapena mphamvu ya Mulungu?+ 25  Chifukwa akufa akadzaukitsidwa, amuna sadzakwatira ndipo akazi sadzakwatiwa, koma adzakhala ngati angelo akumwamba.+ 26  Koma pa mfundo yakuti akufa amaukitsidwa, kodi inu simunawerenge mʼbuku la Mose munkhani yokhudza chitsamba chaminga, kuti Mulungu anamuuza kuti: ‘Ine ndine Mulungu wa Abulahamu, Mulungu wa Isaki ndi Mulungu wa Yakoboʼ?+ 27  Iye ndi Mulungu wa anthu amoyo, osati akufa. Mukulakwitsa kwambiri anthu inu.”+ 28  Mmodzi wa alembi amene anafika nʼkuwamva akutsutsana, anadziwa kuti anawayankha bwino. Choncho anafunsa Yesu kuti: “Kodi lamulo loyamba* ndi liti pa malamulo onse?”+ 29  Yesu anayankha kuti: “Loyamba ndi lakuti, ‘Tamverani Aisiraeli inu, Yehova* Mulungu wathu ndi Yehova* mmodzi. 30  Muzikonda Yehova* Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, moyo wanu wonse, maganizo anu onse ndi mphamvu zanu zonse.’+ 31  Lachiwiri ndi ili, ‘Uzikonda mnzako mmene umadzikondera wekha.’+ Palibe lamulo lina lalikulu kuposa amenewa.” 32  Mlembiyo ananena kuti: “Mphunzitsi, mwanena bwino mogwirizana ndi choonadi, ‘Iye ndi Mmodzi ndipo palibenso Mulungu wina kupatulapo iyeyo.’+ 33  Ndipo kukonda Mulungu ndi mtima wonse, maganizo onse, mphamvu zonse komanso kukonda mnzako mmene umadzikondera wekha, nʼzofunika kwambiri kuposa nsembe zonse zopsereza zathunthu ndi nsembe zina.”+ 34  Yesu atazindikira kuti mlembiyo wayankha mwanzeru, anamuuza kuti: “Iwe suli kutali ndi Ufumu wa Mulungu.” Koma panalibe amene analimba mtima kuti amufunsenso.+ 35  Komabe, pamene Yesu ankaphunzitsa mʼkachisi, ananena kuti: “Nʼchifukwa chiyani alembi amanena kuti Khristu ndi mwana wa Davide?+ 36  Kudzera mwa mzimu woyera,+ Davideyo ananena kuti, ‘Yehova* anauza Ambuye wanga kuti: “Khala kudzanja langa lamanja mpaka nditaika adani ako pansi pa mapazi ako.”’+ 37  Davideyo anamutchula kuti Ambuye, ndiye zingatheke bwanji kuti akhale mwana wake?”+ Ndipo gulu lalikulu la anthu linkamumvetsera mosangalala. 38  Pophunzitsapo Yesu ananenanso kuti: “Chenjerani ndi alembi amene amakonda kuyendayenda atavala mikanjo komanso amakonda kupatsidwa moni mʼmisika.+ 39  Amakondanso kukhala mʼmipando yakutsogolo* mʼmasunagoge komanso mʼmalo olemekezeka kwambiri pachakudya chamadzulo.+ 40  Iwo amalanda chuma cha akazi* amasiye ndipo amapereka mapemphero ataliatali pofuna kudzionetsera.* Anthu amenewa adzalandira chilango chowawa kwambiri.”* 41  Ndiyeno anakhala pansi pamalo amene ankatha kuona moponyeramo zopereka*+ ndipo anayamba kuona mmene gulu la anthu linkaponyera ndalama moponyera zoperekamo. Anaona anthu ambiri olemera akuponyamo makobidi ambiri.+ 42  Kenako panafika mkazi wamasiye wosauka ndipo anaponyamo timakobidi tiwiri tatingʼono, tochepa mphamvu kwambiri.*+ 43  Ndiyeno Yesu anaitana ophunzira ake nʼkuwauza kuti: “Ndithu ndikukuuzani kuti mkazi wamasiye wosaukayu waponya zochuluka kuposa ena onse amene aponya ndalama moponyera zoperekamo.+ 44  Zili choncho chifukwa onsewo aponya zimene atapa pa zochuluka zimene ali nazo, koma mayiyu, mu umphawi wake, waponya zonse zimene anali nazo, inde zonse zimene zikanamuthandiza pa moyo wake.”+

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “mutu wa kona.”
Kapena kuti, “kumumanga.”
Kapena kuti, “nʼzoyenera.”
Kapena kuti, “lofunika kwambiri.”
Kapena kuti, “mʼmipando yabwino kwambiri.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Iwo amadya nyumba za akazi.”
Kapena kuti, “mwachiphamaso.”
Kapena kuti, “champhamvu.”
Kapena kuti, “bokosi la zopereka.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “malepitoni awiri amene anali okwana kwadiransi imodzi.” Onani Zakumapeto B14.