Phunzirani kwa Mphunzitsi Waluso

M’Baibulo muli mfundo zothandiza ndipo zikhoza kugwiritsidwa ntchito kulikonse. Ana ayenera kuphunzira zimene Atate wawo wakumwamba amanena osati zimene anthu ena amanena.

Zimene Ana Amafuna Kwa Makolo Awo

Cholinga cha bukuli ndi chofuna kuthandiza ana komanso amene akuwawerengera bukuli kuti azikambirana momasuka nkhani zofunika.

MUTU

Chifukwa Chake Yesu Anali Mphunzitsi Waluso

Kodi Yesu ankaphunzitsa zinthu zotani? Nanga zomwe ankaphunzitsazo anazitenga kuti?

MUTU

Kalata Yochokera kwa Mulungu

Kalatayi imapezeka m’buku lofunika kwambiri kuposa mabuku ena onse.

MUTU

Amene Anapanga Zinthu Zonse

Ndani analenga mbalame ndi kuziphunzitsa kuimba? Ndani analenga udzu? Ndani anakulenga?

MUTU

Mulungu Ali ndi Dzina Lake

Tonsefe tili ndi mayina. Kodi dzina la Mulungu umalidziwa? N’chifukwa chiyani dzina lake ndi lofunika?

MUTU

“Uyu Ndiye Mwana Wanga”

N’chiyani chinapangitsa Yesu kukhala munthu wapadera kwambiri?

MUTU

Mphunzitsi Waluso Anatumikira Anthu Ena

Kodi umasangalala munthu wina akakupangira chinthu chabwino? Tonse timasangalala, ndipo Mphunzitsi Waluso ankadziwa zimenezi.

MUTU

Kumvera Kudzakuteteza

Ana amaphunzira zinthu kuchokera kwa akuluakulu. Ndipo Mulungu akatiuza kuti tichite zinazake sitiyenera kukaikira ngati zilidi zofunika.

MUTU

Mulungu Ndi Wamkulu Kuposa Aliyense

Pali angelo ena abwino komanso pali ena oipa.

MUTU

Tifunika Kukana Ziyeso

Kodi ungachite chiyani ngati munthu wina atakuuza kuti uchite zinthu zoipa?

MUTU

Yesu Ali ndi Mphamvu Kuposa Ziwanda

Sitiyenera kuopa ziwanda komabe tiyenera kukhala osamala kuti zisatipusitse.

MUTU

Angelo a Mulungu Amatithandiza

Angelo a Mulungu amathandiza anthu omwe amakonda Yehova ndi kumutumikira.

MUTU

Yesu Atiphunzitsa Kupemphera

Mungathe kupemphera kwa Mulungu nthawi iliyonse ndipo iye adzamva mapemphero anu.

MUTU

Amene Anakhala Ophunzira a Yesu

Kodi ophunzira a Yesu anali anthu otani?

MUTU

Chifukwa Chake Tiyenera Kukhululukira Ena

Yesu anafotokoza nkhani pofuna kutiphunzitsa kufunika kokhululukira ena.

MUTU

Phunziro la Kukhala Wokoma Mtima

Mungaphunzire zambiri mu nkhani ya Msamariya wabwino.

MUTU

Kodi Chofunika Kwambiri Ndi Chiyani?

Kodi tingakhale bwanji olemera kwa Mulungu?

MUTU

Mmene Tingakhalire Osangalala

Mphunzitsi Waluso anatchula chinsinsi cha zimene zimapangitsa munthu kukhala wosangalala.

MUTU

Kodi Ndi Bwino Kuchita Ndewu?

Kodi mungatani ngati ndewu itayamba?

MUTU

Kodi Nthawi Zonse Umafuna Kukhala Woyamba?

Kodi Yesu anawauza chiyani ophunzira ake atakangana pofuna kudziwa amene anali woyamba?

MUTU

Kodi Tiyenera Kudzitama Tikachita Zabwino?

Yesu ananena nkhani ya Mfarisi ndi wokhometsa msonkho.

MUTU

Chifukwa Chake Tiyenera Kupewa Bodza

Werengani nkhaniyi kuti mudziwe zimene Yehova anachita ndi Hananiya komanso Safira.

MUTU

Chifukwa Chake Anthufe Timadwala

Kodi zidzatheka kuti nthawi ina anthu azingokhala bwinobwino osadwala?

MUTU

Usakhale Wakuba

Werengani nkhaniyi yomwe ikufotokoza za anthu 4 omwe anatenga zinthu za eniake.

MUTU

Kodi Amene Amachita Zinthu Zoipa Angasinthe?

Tikaona zimene Saulo komanso mzimayi amene anali hule anachita, zimasonyeza kuti anthu oipa akhoza kusintha n’kukhala anthu abwino.

MUTU

Chifukwa Chake Kuchita Zinthu Zabwino Kumavuta

Kodi ukuganiza kuti anthu ochita zoipa angamve bwanji ngati utakana kuchita zimene iwowo akufuna?

MUTU

Kodi Mulungu Wako Ndani?

Anthu amalambira milungu yambiri. Kodi inuyo mungalambire mulungu uti? Zimene achinyamata atatu achiheberi anachita zingatithandize kudziwa zimene tingachite.

MUTU

Kudziwa Amene Uyenera Kumumvera

“Perekani zinthu za Kaisara kwa Kaisara, koma zinthu za Mulungu muzizipereka kwa Mulungu.”

MUTU

Kodi Mapwando Onse Amakondweretsa Mulungu?

Kodi mukudziwa kuti Baibulo limanena za mapwando angapo omwe anthu anachita? Tikhoza kudziwa maganizo a Mulungu Tikawerenga nkhani zokhudza mapwandowa.

MUTU

Zimene Zingatithandize Kuthetsa Mantha

Mphunzitsi Waluso sananene kuti kutumikira Yehova n’kosavuta, koma kuti pali njira imene ingatithandize kukhala olimba mtima.

MUTU

Amene Angatitonthoze

Kodi ungatani ngati wakhumudwa kapena ngati ukuona kuti uli wekhawekha?

MUTU

Mmene Yesu Anatetezedwera

Phunzirani mmene Yehova anatetezera Yesu kwa anthu amene ankafuna kumupha ali mwana.

MUTU

Yesu Angatiteteze

Yesu ali padziko lapansi anasonyeza kuti anali ndi mphamvu zoteteza anthu amene ankamukonda.

MUTU

Kodi Chimachitika ndi Chiyani Tikamwalira?

Kodi muyenera kuopa kufa kapena kuopa anthu omwe anamwalira?

MUTU

Tingauke kwa Akufa

Mulungu anapatsa Yesu mphamvu zoukitsa anthu omwe anamwalira kuphatikizaponso ana.

MUTU

Kodi Ndani Adzauka kwa Akufa? Nanga Adzakhala Kuti?

Kodi Yesu ananena zotani pa nkhani imeneyi?

MUTU

Kukumbukira Yehova ndi Mwana Wake

Yesu anasonyeza otsatira ake njira yapadera yokumbukira zimene Yehova komanso iyeyo anatichitira.

MUTU

Chifukwa Chake Tiyenera Kukonda Yesu

Yesu anapereka moyo wake wangwiro kuti tidzapeze moyo wosatha.

MUTU

Kukondweretsa Mulungu

Mwambi wa m’Baibulo umati: ‘Mwananga, khala wanzeru, ukondweretse mtima wanga.’

MUTU

Ana Amene Amakondweretsa Mulungu

Kodi ndi zinthu ziti zimene mungapange kuti musangalatse Mulungu?

MUTU

Chifukwa Chake Tifunikira Kugwira Ntchito

Ntchito imatithandiza kuti tiziganiza bwino komanso kuti matupi athu akhale amphamvu. Mukhoza kuphunzira kuti muzisangalala pogwira ntchito.

MUTU

Kodi Abale Athu ndi Alongo Athu Ndani?

Kodi anthu omwe si a m’banja lanu angakhalenso abale anu?

MUTU

Mabwenzi Athu Azikhala Okonda Mulungu

“Musasocheretsedwe. Kugwirizana ndi anthu oipa kumawononga makhalidwe abwino.”

MUTU

Kodi Ufumu wa Mulungu Ndi Chiyani? Zimene Tingachite Posonyeza Kuti Tikuufuna

Yesu akadzayamba kulamulira dziko lonse lapansi, adzasintha zinthu zambiri padzikoli.

MUTU

Madzi Anawononga Dziko—Kodi Zidzachitikanso?

Anthu olungama adzakhala padzikoli mpaka kalekale.

MUTU

Zimene Zikutidziwitsa Kuti Aramagedo Ili Pafupi

Zizindikiro zikuonekera kulikonse

MUTU

Ungathe Kukhala M’dziko Latsopano la Mulungu

N’chifukwa chiyani ukufuna kudzala ndi moyo wosatha m’Paradaiso?