Phunzirani kwa Mphunzitsi Waluso
M’Baibulo muli mfundo zothandiza ndipo zikhoza kugwiritsidwa ntchito kulikonse. Ana ayenera kuphunzira zimene Atate wawo wakumwamba amanena osati zimene anthu ena amanena.
Zimene Ana Amafuna Kwa Makolo Awo
Cholinga cha bukuli ndi chofuna kuthandiza ana komanso amene akuwawerengera bukuli kuti azikambirana momasuka nkhani zofunika.
MUTU
Chifukwa Chake Yesu Anali Mphunzitsi Waluso
Kodi Yesu ankaphunzitsa zinthu zotani? Nanga zomwe ankaphunzitsazo anazitenga kuti?
MUTU
Kalata Yochokera kwa Mulungu
Kalatayi imapezeka m’buku lofunika kwambiri kuposa mabuku ena onse.
MUTU
Amene Anapanga Zinthu Zonse
Ndani analenga mbalame ndi kuziphunzitsa kuimba? Ndani analenga udzu? Ndani anakulenga?
MUTU
Mulungu Ali ndi Dzina Lake
Tonsefe tili ndi mayina. Kodi dzina la Mulungu umalidziwa? N’chifukwa chiyani dzina lake ndi lofunika?
MUTU
Mphunzitsi Waluso Anatumikira Anthu Ena
Kodi umasangalala munthu wina akakupangira chinthu chabwino? Tonse timasangalala, ndipo Mphunzitsi Waluso ankadziwa zimenezi.
MUTU
Kumvera Kudzakuteteza
Ana amaphunzira zinthu kuchokera kwa akuluakulu. Ndipo Mulungu akatiuza kuti tichite zinazake sitiyenera kukaikira ngati zilidi zofunika.
MUTU
Tifunika Kukana Ziyeso
Kodi ungachite chiyani ngati munthu wina atakuuza kuti uchite zinthu zoipa?
MUTU
Yesu Ali ndi Mphamvu Kuposa Ziwanda
Sitiyenera kuopa ziwanda komabe tiyenera kukhala osamala kuti zisatipusitse.
MUTU
Angelo a Mulungu Amatithandiza
Angelo a Mulungu amathandiza anthu omwe amakonda Yehova ndi kumutumikira.
MUTU
Yesu Atiphunzitsa Kupemphera
Mungathe kupemphera kwa Mulungu nthawi iliyonse ndipo iye adzamva mapemphero anu.
MUTU
Chifukwa Chake Tiyenera Kukhululukira Ena
Yesu anafotokoza nkhani pofuna kutiphunzitsa kufunika kokhululukira ena.
MUTU
Mmene Tingakhalire Osangalala
Mphunzitsi Waluso anatchula chinsinsi cha zimene zimapangitsa munthu kukhala wosangalala.
MUTU
Kodi Nthawi Zonse Umafuna Kukhala Woyamba?
Kodi Yesu anawauza chiyani ophunzira ake atakangana pofuna kudziwa amene anali woyamba?
MUTU
Kodi Tiyenera Kudzitama Tikachita Zabwino?
Yesu ananena nkhani ya Mfarisi ndi wokhometsa msonkho.
MUTU
Chifukwa Chake Tiyenera Kupewa Bodza
Werengani nkhaniyi kuti mudziwe zimene Yehova anachita ndi Hananiya komanso Safira.
MUTU
Chifukwa Chake Anthufe Timadwala
Kodi zidzatheka kuti nthawi ina anthu azingokhala bwinobwino osadwala?
MUTU
Usakhale Wakuba
Werengani nkhaniyi yomwe ikufotokoza za anthu 4 omwe anatenga zinthu za eniake.
MUTU
Kodi Amene Amachita Zinthu Zoipa Angasinthe?
Tikaona zimene Saulo komanso mzimayi amene anali hule anachita, zimasonyeza kuti anthu oipa akhoza kusintha n’kukhala anthu abwino.
MUTU
Chifukwa Chake Kuchita Zinthu Zabwino Kumavuta
Kodi ukuganiza kuti anthu ochita zoipa angamve bwanji ngati utakana kuchita zimene iwowo akufuna?
MUTU
Kodi Mulungu Wako Ndani?
Anthu amalambira milungu yambiri. Kodi inuyo mungalambire mulungu uti? Zimene achinyamata atatu achiheberi anachita zingatithandize kudziwa zimene tingachite.
MUTU
Kudziwa Amene Uyenera Kumumvera
“Perekani zinthu za Kaisara kwa Kaisara, koma zinthu za Mulungu muzizipereka kwa Mulungu.”
MUTU
Kodi Mapwando Onse Amakondweretsa Mulungu?
Kodi mukudziwa kuti Baibulo limanena za mapwando angapo omwe anthu anachita? Tikhoza kudziwa maganizo a Mulungu Tikawerenga nkhani zokhudza mapwandowa.
MUTU
Zimene Zingatithandize Kuthetsa Mantha
Mphunzitsi Waluso sananene kuti kutumikira Yehova n’kosavuta, koma kuti pali njira imene ingatithandize kukhala olimba mtima.
MUTU
Mmene Yesu Anatetezedwera
Phunzirani mmene Yehova anatetezera Yesu kwa anthu amene ankafuna kumupha ali mwana.
MUTU
Yesu Angatiteteze
Yesu ali padziko lapansi anasonyeza kuti anali ndi mphamvu zoteteza anthu amene ankamukonda.
MUTU
Kodi Chimachitika ndi Chiyani Tikamwalira?
Kodi muyenera kuopa kufa kapena kuopa anthu omwe anamwalira?
MUTU
Tingauke kwa Akufa
Mulungu anapatsa Yesu mphamvu zoukitsa anthu omwe anamwalira kuphatikizaponso ana.
MUTU
Kodi Ndani Adzauka kwa Akufa? Nanga Adzakhala Kuti?
Kodi Yesu ananena zotani pa nkhani imeneyi?
MUTU
Kukumbukira Yehova ndi Mwana Wake
Yesu anasonyeza otsatira ake njira yapadera yokumbukira zimene Yehova komanso iyeyo anatichitira.
MUTU
Chifukwa Chake Tiyenera Kukonda Yesu
Yesu anapereka moyo wake wangwiro kuti tidzapeze moyo wosatha.
MUTU
Kukondweretsa Mulungu
Mwambi wa m’Baibulo umati: ‘Mwananga, khala wanzeru, ukondweretse mtima wanga.’
MUTU
Ana Amene Amakondweretsa Mulungu
Kodi ndi zinthu ziti zimene mungapange kuti musangalatse Mulungu?
MUTU
Chifukwa Chake Tifunikira Kugwira Ntchito
Ntchito imatithandiza kuti tiziganiza bwino komanso kuti matupi athu akhale amphamvu. Mukhoza kuphunzira kuti muzisangalala pogwira ntchito.
MUTU
Kodi Abale Athu ndi Alongo Athu Ndani?
Kodi anthu omwe si a m’banja lanu angakhalenso abale anu?
MUTU
Mabwenzi Athu Azikhala Okonda Mulungu
“Musasocheretsedwe. Kugwirizana ndi anthu oipa kumawononga makhalidwe abwino.”
MUTU
Kodi Ufumu wa Mulungu Ndi Chiyani? Zimene Tingachite Posonyeza Kuti Tikuufuna
Yesu akadzayamba kulamulira dziko lonse lapansi, adzasintha zinthu zambiri padzikoli.
MUTU
Madzi Anawononga Dziko —Kodi Zidzachitikanso?
Anthu olungama adzakhala padzikoli mpaka kalekale.
MUTU
Ungathe Kukhala M’dziko Latsopano la Mulungu
N’chifukwa chiyani ukufuna kudzala ndi moyo wosatha m’Paradaiso?