Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

JW LIBRARY

Mafunso Ofunsidwa Kawirikawiri Okhudza JW Library (Pa Zipangizo za iOS)

Mafunso Ofunsidwa Kawirikawiri Okhudza JW Library (Pa Zipangizo za iOS)

JW Library ingathe kugwira ntchito pa mafoni ndi zipangizo zimene zimayendera mapulogalamu awa:

  • Android 7.0 kapena ina yaposachedwapa

  • iOS 15.0 kapena ina yaposachedwapa

  • Windows 10 ya 1903 ena ina yaposachedwapa

Kuti JW Library ikhale yotetezeka komanso izigwira bwino ntchito, tasiya kuigwiritsa ntchito pa zipangizo zina zonse zoyendera mapulogalamu akale. Nthawi ndi nthawi tizikuuzani kuti JW Library ikufunika mapulogalamu atsopano kuti izigwira bwino ntchito. Choncho tikukulimbikitsani kuti muzionetsetsa kuti foni yanu kapena chipangizo chanu chikuyendera pulogalamu yatsopano kwambiri. Ngati simungakwanitse kuika pulogalamu yogwirizana ndi JW Library pachipangizo chanu, mukhozabe kugwiritsa ntchito JW Library pachipangizocho, koma simuzilandira zinthu zimene zasintha mu JW Library.

 

Mitunduyi ikugwirizana kwambiri ndi magulu 8 a mabuku a m’Baibulo omwe afotokozedwa pa Funso 19, m’kabuku kakuti Kodi M’Baibulo Muli Nkhani Zotani?

 

Vuto: Nditaika JW Library yatsopano, panabwera uthenga wakuti manotsi ndi zinthu zimene ndinachonga zapita. Notsi zonse zimene ndinalemba, matagi, zimene ndinachonga komanso zinthu zina sindingazionenso.

Zimene Mungachite: Ngati mwaika m’chipangizo chanu pulogalamu yatsopano vutoli likhoza kutha. Ikani pulogalamu yatsopano n’kutsatira malangizo amene angabwere pa sikirini kuti notsi ndi zinthu zina zibwerere.

 

Mnzanu yemwe amadziwa bwino JW Library akhoza kukuthandizani. Ngati sangakwanitse kukuthandizani, funsani ku ofesi ya nthambi yathu yomwe ili pafupi.