Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Kumanga Tsogolo Langa na Yehova

Kumanga Tsogolo Langa na Yehova

Daunilodi:

  1. 1. Sembe ningakwanitse kudziŵa za tsogolo langa,

    Ningadziŵe mmene umoyo wanga udzakhalila.

    Ine nidziŵa, olo zivute bwanji

    Nipeleka moyo wanga kwa M’lungu.

    (KOLASI)

    Pa zonse nili nazo pa umoyo wanga,

    Coposa zonse, inde capadela

    Nikukondweletsa M’lungu mwa zosankha zanga.

    Ananipatsa zonse; sinidzaiŵala.

    Amasamala za umoyo wanga

    Nidzatumikila M’lungu kwa umoyo wonse.

  2. 2. Mpata ukaoneka wocita zinthu zolakwika.

    Na kucoka panjila yabwino yopita kumoyo,

    Kukumbukila kudzipeleka kwanga

    Inde, kunganilimbitse kwambili.

    (KOLASI)

    Pa zonse nili nazo pa umoyo wanga,

    Coposa zonse, inde capadela

    Nikukondweletsa M’lungu mwa zosankha zanga.

    Ananipatsa zonse; sinidzaiŵala.

    Amasamala za umoyo wanga

    Nidzatumikila M’lungu kwa umoyo wonse

    (BILIJI)

    Moyo wazoona nikonzekela

    Bwenzi langa M’lungu adzanithandiza

    Moyo weniweni nidzalandila

    Ngati Yehova M’lungu Nim’tsangalatsa.

    (KOLASI)

    Pa zonse nili nazo pa umoyo wanga,

    Coposa zonse, inde capadela

    Nikukondweletsa M’lungu mwa zosankha zanga.

    Ananipatsa zonse; sinidzaiŵala.

    Amasamala za umoyo wanga

    Nidzatumikila M’lungu kwa umoyo wonse

    Nidzatumikila M’lungu kwa umoyo wonse