Wolembedwa ndi Yohane 10:1-42

  • Mʼbusa ndi makola a nkhosa (1-21)

    • Yesu ndi mʼbusa wabwino (11-15)

    • “Ndili ndi nkhosa zina” (16)

  • Ayuda anakumana ndi Yesu ku Chikondwerero Chopereka Kachisi kwa Mulungu (22-39)

    • Ayuda ambiri anakana kukhulupirira (24-26)

    • “Nkhosa zanga zimamva mawu anga” (27)

    • Mwana ndi wogwirizana ndi Atate (30, 38)

  • Anthu ambiri akutsidya la Yorodano anakhulupirira (40-42)

10  “Ndithudi ndikukuuzani, wolowa mʼkhola la nkhosa mochita kukwera pamalo ena, osati kudzera pakhomo, ameneyo ndi wakuba ndiponso wolanda zinthu za ena.+  Koma amene amalowera pakhomo ndi mʼbusa wa nkhosazo.+  Mlonda wapakhomo amamutsegulira+ ndipo nkhosa zimamvera mawu ake.+ Nkhosa zakezo amazitchula mayina nʼkuzitsogolera kutuluka nazo.  Akatulutsa nkhosa zake zonse kunja, amazitsogolera ndipo nkhosazo zimamutsatira, chifukwa zimadziwa mawu ake.  Sizidzatsatira mlendo koma zidzamuthawa, chifukwa sizidziwa mawu a alendo.”  Yesu ananena fanizoli kwa iwo, koma iwo sanamvetse tanthauzo la zimene ankawauzazo.  Choncho Yesu anawauzanso kuti: “Ndithudi ndikukuuzani, ine ndine khomo limene nkhosa zimadutsa.+  Onse amene abwera nʼkumanama kuti ndi abusa enieni, ndi akuba komanso olanda zinthu za ena ndipo nkhosa sizinawamvere.  Ine ndine khomo. Aliyense wolowa kudzera mwa ine adzapulumuka ndipo azidzalowa ndi kutuluka kukapeza msipu.+ 10  Wakuba amabwera ndi cholinga chofuna kudzaba, kudzapha ndi kudzawononga.+ Koma ine ndabwera kuti nkhosa zikhale ndi moyo komanso kuti zikhale nawo wochuluka. 11  Ine ndine mʼbusa wabwino.+ Mʼbusa wabwino amapereka moyo wake chifukwa cha nkhosa.+ 12  Munthu waganyu, amene si mʼbusa ndipo nkhosazo si zake, akaona mmbulu ukubwera amasiya nkhosazo nʼkuthawa. Ndiyeno mmbuluwo umazigwira nʼkuzibalalitsa. 13  Amachita zimenezi chifukwa iye ndi waganyu ndipo sasamala za nkhosazo. 14  Ine ndine mʼbusa wabwino. Nkhosa zanga ndimazidziwa ndipo nazonso zimandidziwa,+ 15  ngati mmene zilili kuti Atate amandidziwa ndipo inenso ndimadziwa Atate.+ Choncho ndikupereka moyo wanga chifukwa cha nkhosazo.+ 16  Ndili ndi nkhosa zina zimene si zamʼkhola ili.+ Zimenezonso ndiyenera kuzibweretsa ndipo zidzamva mawu anga. Zidzakhala gulu limodzi ndipo mʼbusa wawo adzakhala mmodzi.+ 17  Atate amandikonda+ chifukwa chakuti ndikupereka moyo wanga+ kuti ndikaulandirenso. 18  Palibe munthu amene akuchotsa moyo wanga, koma ndikuupereka mwa kufuna kwanga. Ndili ndi mphamvu zoupereka komanso ndili ndi mphamvu zoulandiranso.+ Atate wanga ndi amene anandilamula kuti ndichite zimenezi.”* 19  Apanso Ayuda anagawanika+ chifukwa cha mawu amenewa. 20  Ambiri a iwo ankanena kuti: “Ameneyu ali ndi chiwanda ndipo ndi wamisala. Nʼchifukwa chiyani mukumumvetsera?” 21  Ena ananena kuti: “Amenewa si mawu a munthu wogwidwa ndi chiwanda ayi. Kodi chiwanda chingatsegule maso a anthu osaona?” 22  Pa nthawiyo mu Yerusalemu munachitika Chikondwerero Chopereka Kachisi kwa Mulungu. Inali nyengo yozizira kwambiri 23  ndipo Yesu ankayenda mʼkachisimo mʼkhonde la zipilala la Solomo.+ 24  Kenako Ayuda anamuzungulira nʼkuyamba kumuuza kuti: “Kodi utivutitsa maganizo mpaka liti? Ngati ndiwedi Khristu, tiuze mosapita mʼmbali.” 25  Yesu anawayankha kuti: “Ndakuuzani kale, koma inu simukukhulupirira. Ntchito zimene ine ndikuchita mʼdzina la Atate wanga, zikundichitira umboni.+ 26  Koma inu simukukhulupirira, chifukwa si inu nkhosa zanga.+ 27  Nkhosa zanga zimamva mawu anga. Ine ndimazidziwa ndipo nkhosazo zimanditsatira.+ 28  Ndidzazipatsa moyo wosatha+ ndipo sizidzawonongeka komanso palibe amene adzazitsomphole mʼdzanja langa.+ 29  Nkhosa zimene Atate wanga andipatsa nʼzofunika kuposa zinthu zina zonse, ndipo palibe amene angazitsomphole mʼdzanja la Atate.+ 30  Ine ndi Atate ndife amodzi.”*+ 31  Apanso Ayudawo anatola miyala kuti amugende. 32  Yesu anawauza kuti: “Ndakuonetsani ntchito zambiri zabwino zochokera kwa Atate. Ndiye mukufuna kundigenda chifukwa cha ntchito iti mwa zimenezi?” 33  Ayudawo anamuyankha kuti: “Sitikufuna kukugenda chifukwa cha ntchito yabwino, koma chifukwa chonyoza Mulungu.+ Iwe ndiwe munthu wamba koma ukudziyesa mulungu.” 34  Yesu anawafunsa kuti: “Kodi mʼChilamulo chanu sanalembemo kuti, ‘Ine ndanena kuti: “Inu ndinu milungu”’?*+ 35  Ngati anthu amene anatsutsidwa ndi mawu a Mulungu omwe satha mphamvu, anawatchula kuti ‘milungu,’+ 36  kodi inu mukundiuza ine amene Atate anandiyeretsa nʼkunditumiza mʼdziko kuti, ‘Ukunyoza Mulungu,’ chifukwa ndanena kuti, ‘Ndine Mwana wa Mulunguʼ?+ 37  Ngati sindikuchita ntchito za Atate wanga, musandikhulupirire. 38  Koma ngati ndikuzichita, ngakhale simukundikhulupirira, khulupirirani ntchitozo,+ kuti mudziwe ndi kupitirizabe kudziwa kuti Atate ndi ine ndife ogwirizana.”+ 39  Choncho anayesanso kuti amugwire, koma anawazemba. 40  Iye anawolokanso Yorodano nʼkupita kumene Yohane ankabatizira poyamba+ ndipo anakhala kumeneko. 41  Anthu ambiri anabwera kwa iye nʼkuyamba kunena kuti: “Yohane sanachite chizindikiro chilichonse, koma zonse zimene Yohane ananena zokhudza munthu uyu zinali zoona.”+ 42  Choncho anthu ambiri kumeneko anamukhulupirira.

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “Ndinalandira lamulo limeneli kuchokera kwa Atate wanga.”
Kapena kuti, “ndife ogwirizana.”
Kapena kuti, “ndinu ofanana ndi mulungu.”