Wolembedwa ndi Yohane 16:1-33

  • Ophunzira a Yesu akhoza kuphedwa (1-4a)

  • Ntchito ya mzimu woyera (4b-16)

  • Chisoni cha ophunzira chidzasanduka chisangalalo (17-24)

  • Yesu anagonjetsa dziko (25-33)

16  “Ndakuuzani zinthu zimenezi kuti chikhulupiriro chanu chisathe.  Anthu adzakuchotsani musunagoge.+ Ndipotu nthawi ikubwera pamene aliyense amene adzakupheni+ adzaganiza kuti wachita utumiki wopatulika kwa Mulungu.  Koma adzachita zimenezi chifukwa sakundidziwa komanso sakudziwa Atate.+  Komabe ndakuuzani zinthu zimenezi, kuti nthawi yoti zichitike ikadzafika, mudzakumbukire kuti ndinakuuzani.+ Zinthu zimenezi sindinakuuzeni pachiyambi chifukwa ndinali pamodzi ndi inu.  Tsopano ndikupita kwa amene anandituma,+ koma palibe aliyense wa inu amene akundifunsa kuti, ‘Mukupita kuti?’  Koma chifukwa ndakuuzani zinthu zimenezi, chisoni chadzaza mʼmitima yanu.+  Kunena zoona, ndikupita kuti inu mupindule. Chifukwa ngati sindipita ndiye kuti mthandizi uja+ sabwera kwa inu. Koma ndikapita ndikamutumiza kwa inu.  Ndipo iye akadzabwera adzapereka umboni wotsimikizika kudzikoli wonena za tchimo, za chilungamo komanso za chiweruzo.  Choyamba adzapereka umboni wonena za tchimo,+ chifukwa iwo sakundikhulupirira.+ 10  Kenako adzapereka umboni wonena za chilungamo, chifukwa ine ndikupita kwa Atate ndipo inu simudzandionanso. 11  Pomaliza adzapereka umboni wonena za chiweruzo, chifukwa wolamulira wa dziko lino waweruzidwa.+ 12  Ndidakali ndi zinthu zambiri zoti ndikuuzeni, koma panopo simungathe kuzimvetsa zonsezo. 13  Koma mthandiziyo akadzabwera, amene ndi mzimu wa choonadi,+ adzakutsogolerani mʼchoonadi chonse. Chifukwa sadzalankhula zongoganiza payekha, koma adzalankhula zimene wamva ndipo adzalengeza kwa inu zinthu zimene zikubwera.+ 14  Iyeyo adzandilemekeza,+ chifukwa adzalengeza kwa inu zinthu zimene walandira kuchokera kwa ine.+ 15  Zinthu zonse zimene Atate ali nazo ndi zanga.+ Nʼchifukwa chake ndikunena kuti mthandiziyo adzalengeza kwa inu zinthu zimene walandira kuchokera kwa ine. 16  Kwa kanthawi simudzandionanso,+ ndipo kwa kanthawi mudzandiona.” 17  Atanena zimenezi, ena mwa ophunzira akewo anayamba kufunsana kuti: “Kodi akutanthauza chiyani pamene akutiuza kuti, ‘Kwa kanthawi simudzandionanso ndipo kwa kanthawi mudzandiona,’ komanso kuti, ‘chifukwa ndikupita kwa Atateʼ?” 18  Iwo ankanena kuti: “Kodi akutanthauza chiyani pamene akuti, ‘kwa kanthawiʼ? Sitikudziwa zimene akunena.” 19  Yesu anadziwa kuti akufuna kumufunsa, choncho anawafunsa kuti: “Kodi mukufunsana zimenezi chifukwa ndanena kuti: ‘Kwa kanthawi simudzandiona, komanso kuti kwa kanthawi mudzandionaʼ? 20  Ndithudi ndikukuuzani, mudzagwetsa misozi ndi kulira mofuula, koma dzikoli lidzasangalala. Mudzamva chisoni, koma chisoni chanu adzachisandutsa chimwemwe.+ 21  Mayi akamabereka amazunzika kwambiri chifukwa nthawi yake yafika. Koma mwana akabadwa sakumbukiranso kupweteka konse kuja chifukwa chosangalala kuti munthu wabadwa padziko. 22  Chimodzimodzi inunso, panopa muli ndi chisoni. Koma ndidzakuonaninso ndipo mitima yanu idzasangalala.+ Palibenso amene adzachititse kuti musiye kusangalala. 23  Pa tsiku limenelo simudzandifunsanso mafunso. Ndithudi ndikukuuzani, ngati mungapemphe chilichonse kwa Atate+ mʼdzina langa adzakupatsani.+ 24  Mpaka pano simunapemphepo chilichonse mʼdzina langa. Pemphani ndipo mudzalandira kuti chimwemwe chanu chisefukire. 25  Ndalankhula zimenezi kwa inu mʼmafanizo. Nthawi ikubwera pamene sindidzalankhulanso ndi inu pogwiritsa ntchito mafanizo, koma ndidzakuuzani za Atate momveka bwino. 26  Pa tsikulo mudzapempha kanthu kwa Atate mʼdzina langa. Sindikutanthauza kuti ine ndidzakupempherani ayi. 27  Atatewo amakukondani chifukwa munandikonda+ ndipo mwakhulupirira kuti ine ndinabwera monga nthumwi ya Mulungu.+ 28  Ndinabwera padzikoli ngati nthumwi yochokera kwa Atate. Tsopano ndikuchoka mʼdzikoli ndipo ndikupita kwa Atate.”+ 29  Ophunzira akewo ananena kuti: “Ambuye, tsopano tikumvetsa zimene mukunena chifukwa simukugwiritsa ntchito mafanizo. 30  Tadziwa tsopano kuti inu mukudziwa zinthu zonse ndipo mʼposafunikanso kuti munthu akufunseni mafunso. Pa chifukwa chimenechi tikukhulupirira kuti munachokeradi kwa Mulungu.” 31  Yesu anawayankha kuti: “Kodi panopa mukukhulupirira? 32  Ndithu ndikukuuzani, nthawi ikubwera ndipo yafika kale, pamene nonse mubalalika, aliyense kupita kunyumba kwake ndipo mundisiya ndekha.+ Koma sindikhala ndekha, chifukwa Atate ali ndi ine.+ 33  Ine ndakuuzani zimenezi kuti mukhale mu mtendere chifukwa cha ine.+ Mʼdzikomu mukumana ndi mavuto aakulu, koma limbani mtima. Ine ndaligonjetsa dziko.”+

Mawu a M'munsi