Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo

M’bukuli muli nkhani zofotokoza zimene zinachitika kale komanso zimene zidzachitike m’tsogolo. Muli nkhani yofotokoza nthawi imene zinthu zinalengedwa, Yesu anabadwa ndiponso kuchita utumiki wake komanso yofotokoza nthawi imene Ufumu wa Mulungu udzabwere.

Kalata Yochokera ku Bungwe Lolamulira

Kodi mungagwiritse ntchito bwanji bukuli?

MUTU 1

Mulungu Analenga Kumwamba ndi Dziko Lapansi

Baibulo limati Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi. Koma kodi ukudziwa kuti analenga mngelo uti asanalenge chilichonse?

MUTU 2

Mulungu Analenga Anthu Awiri Oyamba

Mulungu analenga anthu awiri oyamba n’kuiwaika m’munda wa Edeni. Ankafuna kuti iwo abereke ana ndipo kenako dziko lonse likhale paradaiso.

MUTU 3

Adamu ndi Hava Sanamvere Mulungu

M’munda wa Edeni, kodi mtengo umodzi unali wosiyana bwanji ndi mitengo ina? N’chifukwa chiyani Hava anadya zipatso za mtengowo?

MUTU 4

Anakwiya Mpaka Anapha M’bale Wake

Mulungu analandira nsembe ya Abele koma ya Kaini anaikana. Kaini ataona zimenezi, anakwiya kwambiri ndipo anapha Abele.

MUTU 5

Chingalawa cha Nowa

Angelo oipa atakwatira akazi padzikoli anabereka ana amene ankavutitsa anthu. Chiwawa chinali ponseponse. Koma Nowa sankachita nawo zoipa. Iye ankakonda Mulungu komanso ankamumvera.

MUTU 6

Anthu 8 Anapulumuka

Yehova anabweretsa chigumula pogwetsa mvula kwa masiku 40, usana ndi usiku. Nowa ndi banja lake anakhala m’chingalawa kwa nthawi yoposa chaka. Kenako Mulungu anawauza kuti atuluke.

MUTU 7

Nsanja ya ku Babele

Anthu anaganiza zomanga mzinda wokhala ndi nsanja yaitali mpaka kumwamba. N’chifukwa chiyani Mulungu anawapangitsa kuti mwadzidzidzi ayambe kulankhula zinenero zosiyanasiyana?

MUTU 8

Abulahamu ndi Sara Anamvera Mulungu

N’chifukwa chiyani Abulahamu ndi Sara anasiya mzinda wolemera wa Uri n’kumakakhala ngati alendo ku Kanani?

MUTU 9

Anakhala Ndi Mwana Atakalamba

Kodi Mulungu anakwaniritsa bwanji lonjezo lake kwa Abulahamu? Kodi analikwaniritsa kudzera mwa mwana uti, Isaki kapena Isimaeli?

MUTU 10

Kumbukirani Mkazi wa Loti

Mulungu anachititsa kuti moto ndi sulufule zigwere mumzinda wa Sodomu ndi wa Gomora. N’chifukwa chiyani mizindayi inawonongedwa? N’chifukwa chiyani tiyenera kukumbukira mkazi wa Loti?

MUTU 11

Abulahamu Anasonyeza Kuti Anali Wokhulupirika

Mulungu anauza Abulahamu kuti: ‘Chonde, tenga mwana wako mmodzi yekhayo kuti ukamupereke nsembe paphiri la Moriya.’ Kodi pamenepa Abulahamu akanatani?

MUTU 12

Yakobo Analandira Madalitso

Isaki ndi Rebeka anali ndi ana awiri amapasa ndipo mayina awo anali Esau ndi Yakobo. Esau anali wamkulu ndipo ankayenera kulandira madalitso. N’chifukwa chiyani anasinthanitsa madalitsowo ndi mbale ya mphodza?

MUTU 13

Yakobo ndi Esau Anagwirizananso

Kodi Yakobo anatani kuti mngelo amudalitse? Nanga anatani kuti akhululukirane ndi Esau?

MUTU 14

Kapolo Amene Ankamvera Mulungu

Yosefe ankachita zabwino koma anavutika kwambiri. N’chifukwa chiyani?

MUTU 15

Yehova Sanamuiwale Yosefe

Ngakhale kuti Yosefe anali kutali ndi achibale ake, Yehova anali naye.

MUTU 16

Kodi Yobu Anali Ndani?

Yobu ankamvera Yehova ngakhale zinthu zitavuta.

MUTU 17

Mose Anasankha Kuti Azilambira Yehova

Mose ali mwana anapulumuka chifukwa cha nzeru za mayi ake.

MUTU 18

Anaona Chitsamba Chikuyaka

N’chifukwa chiyani chitsamba chinkayaka koma osapsa?

MUTU 19

Miliri Itatu Yoyambirira

Farao anabweretsera anthu ake mavuto chifukwa anali wonyada ndipo anakana kuti anthu a Mulungu apite.

MUTU 20

Miliri Inanso 6

Kodi miliri imeneyi inasiyana bwanji ndi itatu yoyamba ija?

MUTU 21

Mliri wa 10

Mliri umenewu unali wopweteka kwambiri moti Farao analola kuti Aisiraeli apite.

MUTU 22

Pa Nyanja Yofiira Panachitika Zodabwitsa Kwambiri

Farao sanafe ndi miliri 10. Koma kodi anapulumukanso pa chozizwitsa cha pa Nyanja Yofiirachi?

MUTU 23

Analonjeza Kuti Azimvera Yehova

Atafika paphiri la Sinai, Aisiraeli analonjeza Mulungu kuti azimumvera.

MUTU 24

Aisiraeli Sanachite Zimene Analonjeza

Mose ali kokatenga Malamulo 10, Aisiraeli anachimwira Mulungu.

MUTU 25

Chihema Cholambiriramo

Mutenti yapadera imeneyi munkakhala likasa la pangano.

MUTU 26

Anthu 12 Anapita Kukaona Dziko la Kanani

Yoswa ndi Kalebe anali osiyana ndi amuna ena 10 omwe anapita kukaona dziko la Kanani.

MUTU 27

Aisiraeli Ena Anaukira Yehova

Kora, Datani, Abiramu, ndi anthu ena 250 analephera kuzindikira mfundo zofunika zokhudza Yehova.

MUTU 28

Bulu wa Balamu Analankhula

Bulu wa Balamu ankaona mngelo amene Balamuyo sankamuona.

MUTU 29

Yehova Anasankha Yoswa

Malangizo amene Mulungu anapereka kwa Yoswa angatithandizenso ifeyo masiku ano.

MUTU 30

Rahabi Anabisa Aisiraeli Okaona Dziko

Mpanda wa mzinda wa Yeriko unagwa. Koma nyumba ya Rahabi sinagwe ngakhale kuti inali yogundizana ndi mpandawo.

MUTU 31

Yoswa ndi Anthu a ku Gibeoni

Yoswa anapemphera kwa Mulungu kuti dzuwa liime. Kodi Mulungu anamumvera?

MUTU 32

Mtsogoleri Watsopano ndi Azimayi Awiri Olimba Mtima

Yoswa atamwalira, Aisiraeli anayamba kulambira mafano. Zinthu zinayamba kusayenda bwino, koma zinthu zinasintha ndi kubwera kwa Woweruza Baraki, Debora mneneri wamkazi komanso Yaeli

MUTU 33

Rute ndi Naomi

Azimayi awiri amene amuna awo anamwalira akubwerera ku Isiraeli. Mmodzi mwa azimayiwo dzina lake Rute anayamba kumakunkha m’minda ya anthu ndipo Boazi anamuona kuti anali wolimbikira ntchito.

MUTU 34

Gidiyoni Anagonjetsa Amidiyani

Amidiyani atayamba kuzunza Aisiraeli, Aisiraeliwo anapempha Yehova kuti awathandize. Kodi zinatheka bwanji kuti asilikali ochepa a Gideoni agonjetse gulu la asilikali okwana 135,000?

MUTU 35

Hana Anapempha Kuti Mulungu Amupatse Mwana Wamwamuna

Elikana anatenga Hana komanso Penina ndi ana ake n’kupita nawo kuchihema ku Silo. Kumeneko Hana anapempha Mulungu kuti amupatse mwana wamwamuna. Patatha chaka anabereka Samueli.

MUTU 36

Zimene Yefita Analonjeza

Kodi Yefita analonjeza chiyani? N’chifukwa chiyani analonjeza? Kodi mwana wake anachita chiyani atamva lonjezolo?

MUTU 37

Yehova Analankhula ndi Samueli

Eli anali Mkulu wa Ansembe ndipo ana ake awiri analinso ansembe. Ana akewa sankamvera malamulo a Mulungu. Koma Samueli ankachita zabwino ndipo tsiku lina Yehova analankhula naye.

MUTU 38

Yehova Anapatsa Mphamvu Samisoni

Yehova anapatsa Samisoni mphamvu kuti agonjetse Afilisiti koma iye atalakwitsa zinthu zina Afilisitiwo anamugwira.

MUTU 39

Mfumu Yoyamba ya Aisiraeli

Mulungu anapatsa Aisiraeli oweruza oti aziwatsogolera koma iwo anapempha kuti akhale ndi mfumu. Samueli anadzoza Sauli kuti akhale mfumu yoyamba koma kenako Yehova anakana Sauliyo. Kodi mukudziwa chifukwa chake?

MUTU 40

Davide Anapha Goliyati

Yehova anasankha Davide kuti adzakhale mfumu yotsatira ya Aisiraeli, ndipo zimene Davide anachita zinasonyeza kuti Yehova anasankha bwino.

MUTU 41

Davide ndi Sauli

N’chifukwa chiyani Sauli ankadana ndi Davide, nanga Davideyo anatani?

MUTU 42

Yonatani Anali Wolimba Mtima Komanso Wokhulupirika

Mwana wa mfumu anakhala mnzake wapamtima wa Davide.

MUTU 43

Tchimo la Mfumu Davide

Zimene Davide anachita zinabweretsa mavuto aakulu.

MUTU 44

Kachisi wa Yehova

Mulungu anayankha pemphero la Solomo ndipo anamupatsa zinthu zambiri.

MUTU 45

Ufumu Unagawikana

Aisiraeli ambiri anasiya kutumikira Yehova

MUTU 46

Zimene Zinachitika Paphiri la Karimeli

Kodi Mulungu woona ndi ndani? Yehova kapena Baala?

MUTU 47

Yehova Analimbikitsa Eliya

Kodi mukuganiza kuti nanunso angakulimbikitseni?

MUTU 48

Mwana wa Mzimayi Wamasiye Anaukitsidwa

M’nyumba mwa mzimayi wamasiye munachitika zozizwitsa ziwiri

MUTU 49

Yehova Anapereka Chilango kwa Mfumukazi Yoipa

Yezebeli anakonza zoti Mwisiraeli wotchedwa Naboti aphedwe n’cholinga choti alande munda wake. Koma Yehova Mulungu anaona zinthu zopanda chilungamozi

MUTU 50

Yehova Anathandiza Mfumu Yehosafati

Yehosafati anali mfumu yabwino ndipo adani ataukira Yuda, iye anapemphera kwa Mulungu kuti amuthandize.

MUTU 51

Kamtsikana Kanathandiza Mkulu wa Asilikali

Kamtsikana kachiisiraeli kanauza abwana ake aakazi kuti Yehova ali ndi mphamvu zochiritsa.

MUTU 52

Gulu Lamphamvu la Asilikali a Yehova

Kodi mtumiki wa Elisa anadziwa bwanji kuti ‘panali ambiri amene anali kumbali yawo kuposa amene anali kumbali ya adani awo’?

MUTU 53

Yehoyada Anali Wolimba Mtima

Wansembe wokhulupirika analimbana ndi mfumukazi yoipa.

MUTU 54

Yehova Anamulezera Mtima Yona

Kodi zinatani kuti mneneri wina wa Mulungu amezedwe ndi chinsomba? Nanga anatuluka bwanji m’mimba mwa chinsombacho? Kodi Yehova anamuphunzitsa chiyani?

MUTU 55

Mngelo wa Yehova anateteza Hezekiya

Adani a Ayuda ankanena kuti Yehova sangathandize anthu ake, koma zimenezi sizinali zoona.

MUTU 56

Yosiya Ankakonda Chilamulo cha Mulungu

Yosiya anakhala mfumu ya Ayuda ali ndi zaka 8, ndipo anathandiza anthu ake kuti azilambira Yehova.

MUTU 57

Yehova Anauza Yeremiya Kuti Azilalikira

Zimene mneneri wachinyamatayu anafotokoza zinakwiyitsa kwambiri akuluakulu a Ayuda.

MUTU 58

Mzinda wa Yerusalemu Unawonongedwa

Ayuda anapitiriza kulambira milungu yonyenga choncho Yehova anawasiya.

MUTU 59

Anyamata 4 Anamvera Yehova

Anyamata achiyuda anakhalabe okhulupirika kwa Yehova ngakhale pamene anali kunyumba yachifumu ku Babulo.

MUTU 60

Ufumu Umene Udzalamulire Mpaka Kalekale

Danieli anafotokoza tanthauzo la maloto odabwitsa a Nebukadinezara.

MUTU 61

Anakana Kulambira Fano

Sadirake, Mesake ndi Abedinego anakana kulambira fano la golide la mfumu ya ku Babulo.

MUTU 62

Ufumu Wofanana ndi Mtengo Waukulu

Maloto a Nebukadinezara anali okhudza tsogolo lake.

MUTU 63

Dzanja Linalemba Pakhoma

Kodi dzanjali linalemba pakhoma pa nthawi iti ndipo zinkatanthauza chiyani?

MUTU 64

Danieli Anaponyedwa M’dzenje la Mikango

Tizipemphera kwa Yehova tsiku lililonse ngati Danieli.

MUTU 65

Esitere Anapulumutsa Anthu a Mtundu Wake

Ngakhale kuti iye anali mlendo m’dzikoli komanso wamasiye anakhala mfumukazi.

MUTU 66

Ezara Ankaphunzitsa Chilamulo cha Mulungu

Aisiraeli atamvetsera zimene Ezara anawawerengera, anapanga lonjezo lapadera kwa Mulungu.

MUTU 67

Mpanda wa Yerusalemu Unamangidwanso

Nehemiya anamva zoti adani akufuna kuwaukira. N’chifukwa chiyani iye sanaope?

MUTU 68

Elizabeti Anakhala ndi Mwana

N’chifukwa chiyani mwamuna wa Elizabeti anauzidwa kuti sadzalankhula mpaka mwana atabadwa?

MUTU 69

Gabirieli Anaonekera kwa Mariya

Anamuuza uthenga womwe unasintha moyo wake.

MUTU 70

Angelo Analengeza za Kubadwa kwa Yesu

Angelo atangomva za kubadwa kwa Yesu ananyamuka nthawi yomweyo.

MUTU 71

Yehova Anateteza Yesu

Mfumu yoipa inkafuna kupha Yesu.

MUTU 72

Zimene Yesu Anachita Ali Wamng’ono

Kodi Yesu anachita chiyani kukachisi, zomwe zinadabwitsa aphunzitsi?

MUTU 73

Yohane Anakonza Njira

Yohane atakula anakhala mneneri. Iye ankaphunzitsa kuti Mesiya akubwera. Kodi anthu ankatani akamva uthenga wake?

MUTU 74

Yesu Anakhala Mesiya

Kodi Yohane ankatanthauza chiyani pamene ananena kuti Yesu ndi Mwanawankhosa wa Mulungu?

MUTU 75

Mdyerekezi Anayesa Yesu

Mdyerekezi anayesa Yesu katatu. Kodi mayesero ake anali otani? Kodi Yesu anatani?

MUTU 76

Yesu Anayeretsa Kachisi

N’chifukwa chiyani Yesu anatulutsa nyama m’kachisi ndiponso anagubuduza matebulo a osintha ndalama?

MUTU 77

Yesu Anakumana ndi Mayi Pachitsime

N’chifukwa chiyani mayi wachisamariya anadabwa kuona kuti Yesu akumulankhula? Kodi Yesu anamuuza mfundo iti yomwe anali asanauze aliyense?

MUTU 78

Yesu Ankalalikira Uthenga wa Ufumu

Yesu anauza ophunzira ake kuti akhala “asodzi a anthu.” Kenako anaphunzitsa ophunzira ake 70 kuti azikalalikira uthenga wabwino.

MUTU 79

Yesu Anachita Zozizwitsa Zambiri

Kulikonse kumene Yesu ankapita, kunkakhala anthu odwala oti awathandize ndipo iye ankawachiritsa. Ndiponso anaukitsa kamtsikana kena.

MUTU 80

Yesu Anasankha Atumwi 12

Kodi Yesu anawasankhiranji? Kodi mukukumbukira mayina awo?

MUTU 81

Ulaliki wa Paphiri

Yesu anaphunzitsa anthu zinthu zothandiza kwambiri.

MUTU 82

Yesu Anaphunzitsa Otsatira Ake Kupemphera

Kodi iye anawauza kuti ‘azipemphabe’ zinthu ziti?

MUTU 83

Yesu Anadyetsa Anthu Ambiri

Kodi chozizwitsa chimenechi chikutiuza chiyani za Yehova ndi Yesu?

MUTU 84

Yesu Anayenda Panyanja

Kodi mukuganiza kuti atumwi anamva bwanji ataona chozizwitsa chimenechi?

MUTU 85

Yesu Anachiritsa Munthu pa Tsiku la Sabata

N’chifukwa chiyani anthu ena sanasangalale ndi zimene Yesu anachita?

MUTU 86

Yesu Anaukitsa Lazaro

Yesu ataona Mariya akulira, nayenso analira. Koma kenako chisoni chawo chinasanduka chisangalalo.

MUTU 87

Chakudya Chamadzulo Chomaliza

Yesu anapereka malangizo ofunika kwambiri kwa atumwi ake pa nthawi ya chakudya chamadzulo chomaliza.

MUTU 88

Yesu Anamangidwa

Yudasi Isikariyoti anatsogolera gulu la anthu lonyamula malupanga komanso zibonga kumunda wa Getsemani kuti akagwire Yesu.

MUTU 89

Petulo Anakana Yesu

Kodi chinachitika n’chiyani pabwalo pa nyumba ya Kayafa? Nanga n’chiyani chinkachitikira Yesu mkati mwa nyumbayo?

MUTU 90

Yesu Anaphedwa ku Gologota

N’chifukwa chiyani Pilato analamula kuti Yesu aphedwe?

MUTU 91

Yesu Anaukitsidwa

Kodi ndi zinthu zodabwitsa ziti zimene zinachitika pa masiku angapo pambuyo pa imfa ya Yesu?

MUTU 92

Yesu Anakumana ndi Asodzi

Kodi anachita chiyani kuti ayambe kukambirana nawo?

MUTU 93

Yesu Anabwerera Kumwamba

Koma asanabwerere kumwamba anapereka malangizo ofunika kwambiri kwa ophunzira ake.

MUTU 94

Ophunzira a Yesu Analandira Mzimu Woyera

Kodi mzimu woyera unawapatsa mphamvu yodabwitsa yotani?

MUTU 95

Sanasiye Kulalikira

Atsogoleri achipembedzo amene anapha Yesu ankayesetsa kuletsa ophunzira ake kuti asamalalikire. Koma ophunzirawo sanasiye kulalikira.

MUTU 96

Yesu Anasankha Saulo

Saulo ankachitira nkhanza Akhristu koma anasintha.

MUTU 97

Koneliyo Analandira Mzimu Woyera

N’chifukwa chiyani Mulungu anatumiza Petulo kunyumba ya munthuyu yemwe sanali Myuda?

MUTU 98

Anthu a Mitundu Ina Anamva Uthenga Wabwino

Mtumwi Paulo ndi amishonale anzake anayamba kulalikira kumayiko akutali.

MUTU 99

Woyang’anira Ndende Anaphunzira Mawu a Yehova

Zinthu zina zimene zikutchulidwa mu nkhaniyi ndi chiwanda, chivomezi komanso lupanga.

MUTU 100

Paulo ndi Timoteyo

Anthu awiriwa akatumikira Mulungu limodzi mogwirizana kwa zaka zambiri.

MUTU 101

Paulo Anatumizidwa ku Roma

Ngakhale kuti ulendo wake unali woopsa palibe chilichonse chimene chinalepheretsa mtumwi Paulo pa ulendowo.

MUTU 102

Zimene Yohane Anaona M’masomphenya

Yesu anaonetsa Yohane masomphenya a zimene zidzachitike m’tsogolo.

MUTU 103

“Ufumu Wanu Ubwere”

Zimene Yohane anaona zimasonyeza kuti Ufumu wa Mulungu udzasintha kwambiri zinthu padzikoli.