Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

GALAMUKA! Na. 2 2018 | Zinsinsi 12 za Banja Lacimwemwe

Zinsinsi 12 za Mabanja Acimwemwe

Timamva zifukwa zosiyana-siyana zimene zimapangitsa mabanja kupasuka.

  • M’zaka za pakati pa 1990 ndi 2015, ciŵelengelo ca osudzulana ku America cinawonjezeka kuwilikiza kaŵili kwa anthu a zaka zopitilila 50. Ndipo a zaka zopitilila 65 ciŵelengelo cawo cinawilikiza katatu.

  • Akatswili ena amalimbikitsa makolo kuti nthawi zonse aziyamikila ana awo. Enanso amakamba kuti azilanga ana awo mwamphamvu na colinga cofuna kuwathandiza. Conco, makolo sadziŵa zimene angacite.

  • Acicepele amakula, koma osadziŵa maluso ofunikila kuti akhale na umoyo wabwino.

Nanga cimathandiza mabanja ena kukhala acimwemwe n’ciani? Zoona n’zakuti . . .

  • Ukwati ungakhale wokondweletsa komanso mgwilizano wa moyo wonse.

  • Makolo angaphunzile kupeleka cilango mwacikondi kwa ana awo.

  • Acicepele angaphunzile maluso amene angafunikile akadzakula.

Motani? Magazini ino ya Galamuka! idzafotokoza zinsinsi 12 za mabanja acimwemwe.

 

1: Kukhulupilika

Zinthu zitatu zimene zingathandize okwatilana kukhalabe ogwilizana.

2: Kugwilizana

Kodi mnzanu wa m’cikwati mumamuona monga munthu wokhala naye nyumba imodzi cabe?

3: Kulemekezana

Dziŵani zofunika kukamba komanso kucita kuti mnzanu wa m’cikwati azidzimva wolemekezedwa.

4: Kukhululukilana

Kodi mungacite ciani kuti musamasumike kwambili maganizo anu pa zimene mnzanu wa m’cikwati amalakwitsa?

5: Kukambilana

Masitepu atatu amene angakuthandizeni kukhala pa ubwenzi wolimba ndi ana anu.

6: Cilango

Kodi kupeleka cilango kwa mwana kumam’pangitsa kudziona wosafunika?

7: Makhalidwe

Kodi muyenela kuphunzitsa ana anu mfundo zabwanji?

8: Citsanzo

Ngati mufuna kuti mau anu aziwafika pamtima ana anu, mufunika kucita zinthu mogwilizana na zimene mumakamba.

9: Umunthu Wanu

Kodi acicepele angakhalile bwanji kumbuyo zimene amakhulupilila?

10: Kudalilika

Kudalilidwa na makolo ni sitepu yofunika kuti mukhale wokhwima m’maganizo.

11: Kukhala Wolimbika

Kuphunzila kugwila nchito molimbika muli wacicepele kungakuthandizeni pa zilizonse zimene mucita mu umoyo.

12: Zolinga

Kukwanilitsa zolinga kungakuthandizeni kukhala na cidalilo, kulimbitsa maubwenzi anu, ndiponso kuonjezela cimwemwe canu.

12: Zolinga

Kukwanilitsa zolinga kungakuthandizeni kukhala na cidalilo, kulimbitsa maubwenzi anu, ndiponso kuonjezela cimwemwe canu.