Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

Dziko Latsopano Lili Pafupi

Dziko Latsopano Lili Pafupi

Pangani Dawunilodi:

  1. 1.Mbalametu zikuimba,

    Mitambo ikuyenda.

    Mukudutsa pachidikha

    Ndipo dzuwa likuwalanso.

    Akufa akuuka,

    Ngati mukungolota.

    Dziko la Paradaiso

    Linalidi pafupi.

  2. 2.Muchidikha muli nyumba

    Ina ili pa phiri.

    Anthu akuimba nyimbo

    Mumtsinje madzi akuyenda.

    Mbewu zachanso m’minda.

    Ndi nthawi yokolora.

    Dziko lokongolali

    Linalidi pafupi.

    (VESI LOKOMETSERA)

    Tiziuza anzathunso

    Zomwe tikuyembekeza.

    Sikudzakhala kulira.

    Zinthu zonse n’zatsopano.

  3. 3.Anthu akusangalala

    Kafungo ka zomera.

    Mukuitanitsa ‘nzanu

    Pamene tsiku likuyamba.

    Tikuthokoza Yehova,

    Posonyeza chikondi.

    Madalitso onsewa

    Analidi pafupi.

    (VESI LOKOMETSERA)

    Ndikaona nkhope yanu,

    Ikumandimwetulira.

    Sindinkaganiza n’komwe

    Kuti tidzakumananso.

  4. 4.Dziko latsopano

    Ndikuliyembekeza.

    Ndi lonjezo la Yehova.

    Ndipo lidzakwaniritsidwa.

    Ndikaganizira izi

    Sindimadanso nkhawa.

    Chifukwatu dzikolo,

    Lilitu pafupi zedi.