Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

Ndife Banja Limodzi

Ndife Banja Limodzi

Pangani Dawunilodi:

  1. 1. Tafika mu dziko lina

    Tachokeratu kutali

    Kuno sikwathu

    Koma Yehova

    Akutithandizadi.

    Ntchitoyi ingativute ndithu,

    Koma ndi ya Yehova.

    Timakondanso abale ndi mtima wonse,

    Tikunena kuti:

    (KOLASI)

    Tonse ndi a Yehova

    Ndifedi banja limodzi

    Kwanu kutalike bwanji,

    Ndifedi

    Banja limodzi.

  2. 2. Mwatichingamira ndithu,

    Mwatilandilatu bwino.

    Nyimbo zayamba pa msokhanowu,

    Chikondi chikukula.

    Tikudziwa ndi Yehova yekha

    Angachititse izi.

    Tim’tamande, timukonde mpaka kale

    Ku madera onse.

    (KOLASI)

    Tonse ndi a Yehova

    Ndifedi banja limodzi

    Kwanu kutalike bwanji,

    Ndifedi

    Banja limodzi.

  3. 3. Mu ndege, tadutsa nyanja

    Kuno tafika n’kutali.

    Tilalikire, anthu abwino

    Omwe tawapezawa.

    Tikumva ngatitu tili kwathu

    N’chikondi cha abale.

    Timakonda ubale wa padziko lonse,

    Kuli konseko.

    (VESI LOKOMETSERA)

    Tikudziwa

    Timakapeza ’bale kulikonse,

    Mali mpaka Mexico,

    Japan mpaka Jamaica.

    (KOLASI)

    Tonse ndi a Yehova

    Ndifedi banja limodzi

    Kwanu kutalike bwanji,

    Ndifedi

    Banja limodzi.

    Ndife mitundu yonse​—

    Ndifedi banja limodzi.

    Timakondana kwambiri

    Tilitu m’banja la Yehova!

    Fiji, Tahiti, ndi New Caledonia;

    Navajo, Blackfoot, ndi Cherokee;

    Azerbaijan, Kazakhstan, ndi Estonia​—

    Ndifedi banja limodzi.